Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 4:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Namnyamula, napita naye kwa amace. Ndipo anakhala pa maondo ace kufikira usana, namwalira.

21. Ndipo anakwera, namgoneka pa kama wa munthu wa Mulungu, naturuka, namtsekera.

22. Naitana mwamuna wace, nati, Nditumizire mmodzi wa anyamata ndi buru mmodzi, kuti ndithamangire kwa munthu uja wa Mulungu, ndi kubweranso.

23. Ndipo anati, Ulikumuka kwa iye lero cifukwa ninji? ngati mwezi wakhala, kapena: mpa sabata? Koma anati, Kuli bwino.

24. Pamenepo anamangirira buru mbereko, nati kwa mnyamata wace, Kusa, tiye; usandilezetsa kuyendaku, ndikapanda kukuuza.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 4