Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 3:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo ici cidzapepuka pamaso pa Yehova; adzaperekanso Amoabu m'dzanja lanu.

19. Ndipo mudzakantha midzi yonse ya matioga, ndi midzi yonse yosankhika, ndi kulikha mitengo yonse yabwino, ndi kufotsera zitsime zonse zamadzi, ndi kuipitsa pa nthaka ponse pabwino ndi miyala.

20. Ndipo kunacitika m'mawa, pomapereka nsembe yaufa, taonani, anafika madzi odzera ku Edomu; ndipo dziko linadzala ndi madzi.

21. Atamva tsono Amoabu onse kuti adakwera mafumu aja kuthirana nao nkhondo, anamemeza onse akumanga lamba m'cuuno ndi okulapo, naima iwo m'malire.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 3