Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 3:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma tsopano, nditengereni wanthetemya. Ndipo kunali, waothetemyayo ali ciyimbire, dzanja la Yehova linamgwera.

16. Ndipo anati, Atero Yehova, Kumbani m'cigwa muno mukhale maenje okha okha.

17. Pakuti atero Yehova, Simudzaona mphepo, kapena kuona mvula, koma cigwaco cidzadzala ndi madzi; ndipo mudzamwa inu, ndi ng'ombe zanu, ndi zoweta zanu.

18. Ndipo ici cidzapepuka pamaso pa Yehova; adzaperekanso Amoabu m'dzanja lanu.

19. Ndipo mudzakantha midzi yonse ya matioga, ndi midzi yonse yosankhika, ndi kulikha mitengo yonse yabwino, ndi kufotsera zitsime zonse zamadzi, ndi kuipitsa pa nthaka ponse pabwino ndi miyala.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 3