Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 24:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Koma mfumu ya Aigupto sinabwerezanso kuturuka m'dziko lace, pakuti mfumu ya Babulo idalanda kuyambira ku mtsinje wa Aigupto kufikira ku mtsinje Firate, ndilo lonse anali nalo mfumu ya Aigupto.

8. Yoyakini anali wa zaka khumi mphambu zisanu ndi zitatu polowa iye ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu miyezi itatu; ndi dzina la mace ndiye Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.

9. Nacita iye coipa pamaso pa Yehova, monga umo monse adacita atate wace.

10. Nthawi ija anyamata a Nebukadinezara mfumu ya Babulo anakwerera Yerusalemu, naumangira mudziwo misasa.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 24