Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 24:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Masiku ace Nebukadinezara mfumu ya ku Babulo anakwerako, Yoyakimu nagwira mwendo wace zaka zitatu; pamenepo anatembenuka nampandukira.

2. Ndipo Yehova anamtumizira magulu a Akasidi, ndi magulu a Aaramu, ndi magulu a Amoabu, ndi magulu a ana a Amoni, nawatumiza pa Yuda kuliononga, monga mwa mau a Yehova: adawanena ndi dzanja la atumiki ace aneneriwo.

3. Zedi ici cinadzera Yuda mwa lamulo la Yehova, kuwacotsa pamaso pace, cifukwa ca zolakwa za Manase, monga mwa zonse anazicita;

4. ndiponso cifukwa ca mwazi wosacimwa adaukhetsa; popeza anadzaza Yerusalemu ndi mwazi wosacimwa; ndipo Yehova sanafuna kukhululukira.

5. Macitidwe ena tsono a Yoyakimu, ndi zonse anazicita, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 24