Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 22:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yosiya ndiye wa zaka zisanu ndi zitatu polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu cimodzi m'Yerusalemu; ndi dzina la mace ndi Yedida mwana wa Adaya wa ku Bozikati.

2. Nacita iye zoongoka pamaso pa Yehova, nayenda m'njira yonse ya Davide kholo lace, osapambukira ku dzanja lamanja kapena kulamanzere.

3. Ndipo kunali caka cakhumi mphambu zisanu ndi zitatu ca Yosiya, mfumuyi inatuma Safani mwana wa Azaliya mwana wa Mesulamu, mlembi, ku nyumba ya Yehova, ndi kuti,

4. Kwera kwa Hilikiya mkulu wa ansembe, awerenge ndalama zimene anthu anabwera nazo ku nyumba ya Yehova, ndizo zimene olindira pakhomo anasonkhetsa anthu; azipereke m'dzanja anchito akuyang'anira nyumba ya Yehova;

5. iwo azipereke kwa ogwira nchito ya m'nyumba ya Yehova, akonze mogamuka nyumbayi,

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 22