Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 21:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri polowa iye ufumu wace, nakhala mfumu zaka makumi asanu ndi zisanu m'Yerusalemu; ndi dzina la mace ndiye Hefisiba.

2. Ndipo anacita coipa pamaso pa Yehova, monga mwa zonyansa za amitundu amene Yehova anawaingitsa pamaso pa ana a Israyeli.

3. Pakuti anamanganso misanje, imene Hezekiya atate wace adaiononga; nautsira Baala maguwa a nsembe, nasema cifanizo, monga anacita Ahabu mfumu ya Israyeli, nagwadira khamu lonse la kuthambo, nalitumikira.

4. Namanga iye maguwa a nsembe m'nyumba ya Yehova imene Yehova adainenera kuti, M'Yerusalemu ndidzaika dzina langa.

5. Nalimangira khamu lonse la kuthambo maguwa a nsembe m'mabwalo awiri a nyumba ya Yehova.

6. Napititsa mwana wace pamoto, naombeza maula, nacita zanyanga, naika obwebweta ndi openda; anacita zoipa zambiri pamaso pa Yehova kuutsa mkwiyo wace.

7. Ndipo anaika cifanizo cosema cimene adacipanga m'nyumba ija Yehova adainenera kwa Davide ndi kwa Solomo mwana wace kuti, M'nyumba muno ndi m'Yerusalemu umene ndausankha mwa mafuko onse a Israyeli ndidzaikamo dzina langa kosatha.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 21