Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 20:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo kunali, asanaturukire Yesaya m'kati mwa mudzi, anamdzera mau a Yehova, ndi kuti,

5. Bwerera, nunene kwa Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga, Atero Yehova Mulungu wa Davide kholo lako, Ndamva pemphero lako, ndapenya misozi yako; taona, nelidzakuciritsa, tsiku lacitatu udzakwera kumka ku nyumba ya Yehova.

6. Ndipo ndakuonjezera pa masiku ako zaka khumi ndi zisanu; ndidzakupulumutsa iwe ndi mudzi uno m'dzanja la mfumu ya Asuri; ndidzacinjiriza mudzi uno, cifukwa ca Ine ndekha, ndi cifukwa ca Davide mtumiki wanga.

7. Nati Yesaya, Tenga ncinci yankhuyu. Naitenga, naiika papfundo, nacira iye.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 20