Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 18:27-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Koma kazembeyo ananena nao, Ngati mbuyanga ananditumiza kwa mbuyako, ndi kwa iwe, kunena mau awa? si kwa anthu awa nanga okhala palinga, kuti akadye zonyansa zao, ndi kumwa mkodzo wao pamodzi ndi inu?

28. Naima kazembeyo, napfuula ndi mau akulu m'Ciyuda, nanena kuti, Tamverani mau a mfumu yaikuru mfumu ya Asuri.

29. Itero mfumu, Asakunyengeni Hezekiya; pakuti sadzakhoza kukulanditsani m'dzanja lace;

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 18