Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 17:37-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. ndi malemba, ndimaweruzo, ndi cilamulo, ndi coikika anakulemberani muzisamalira kuzicita masiku onse, nimusamaopa milungu: yina;

38. ndi cipangano ndinacicita nanu musamaciiwala, kapena kuopa milungu yina iai;

39. koma Yehova Mulungu wanu muzimuopa, nadzakulanditsani Iyeyu m'dzanja la adani anu onse.

40. Koma sanamvera, nacita monga mwa mwambo wao woyamba.

41. Ndipo amitundu awa anaopa Yehova, natumikira mafano ao osema; ana ao omwe, ndi zidzukulu zao zomwe, monga anacita makolo ao, momwemo iwo omwe mpaka lero lino.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 17