Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 17:35-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. ndiwo amene Yehova adapangana nao, nawalamulira, ndi kuti, Musamaopa milungu yina, kapena kuigwadira, kapena kuitumikira, kapena kuiphera nsembe;

36. koma Yehova amene anakukwezani kukuturutsani m'dziko la Aigupto ndi mphamvu yaikuru, ndi dzanja lotambasuka, Iyeyu muzimuopa, ndi Iyeyu muzimgwadira, ndi Iyeyu muzimphera nsembe;

37. ndi malemba, ndimaweruzo, ndi cilamulo, ndi coikika anakulemberani muzisamalira kuzicita masiku onse, nimusamaopa milungu: yina;

38. ndi cipangano ndinacicita nanu musamaciiwala, kapena kuopa milungu yina iai;

39. koma Yehova Mulungu wanu muzimuopa, nadzakulanditsani Iyeyu m'dzanja la adani anu onse.

40. Koma sanamvera, nacita monga mwa mwambo wao woyamba.

41. Ndipo amitundu awa anaopa Yehova, natumikira mafano ao osema; ana ao omwe, ndi zidzukulu zao zomwe, monga anacita makolo ao, momwemo iwo omwe mpaka lero lino.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 17