Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 15:36-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Macitidwe ena tsono a Yotamu, ndi zonse anazicita, sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

37. Masiku awa Yehova anayamba kutumizira Yuda Rezini mfumu ya Aramu, ndi Peka mwana wa Remaliya, amenyane naye.

38. Ndipo anagona Yotamu ndi makolo ace, namuika pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Davide kholo lace; nakhala mfumu m'malo mwace Ahazi mwana wace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 15