Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 14:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Pakuti Yehova anapenya kuti kuzunzika kwao kwa Israyeli nkowawa ndithu; popeza panalibe womangika kapena womasuka, ndipo panalibe womthandiza Israyeli.

27. Ndipo Yehova sadanena kuti adzafafaniza dzina la Israyeli pansi pa thambo; koma anawapulumutsa ndi dzanja la Yerobiamu mwana wa Yoasi.

28. Macitidwe ena tsono a Yerobiamu, ndi zonse anazicita, ndi mphamvu yace, umo anacita nkhondo, nabweza kwa Israyeli Damasiko ndi Hamati amene anali a Yuda, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

29. Ndipo Yerobiamu anagona ndi makolo ace, ndiwo mafumu a Israyeli; nakhala mfumu m'malo mwace Zekariya mwana wace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 14