Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 14:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka caciwiri ca Yoasi mwana wa Yoahazi mfumu ya Israyeli, Amaziya mwana wa Yoasi mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.

2. Ndiye wa zaka makumi awiri ndi zisanu polowa ufumu; nakhala mfumu zaka makumi awiri mphambu zisanu ndi zinai m'Yerusalemu; dzina la mace ndiye Yoadana wa ku Yerusalemu.

3. Ndipo anacita zoongoka pamaso pa Yehova, koma wosanga Davide kholo lace; nacita monga mwa zonse anazicita Yoasi atate wace.

4. Koma misanje sanaicotsa; anthu anapherabe nsembe, nafukiza pamisanje.

5. Ndipo kunali, utakhazikika ufumu m'dzanja lace, anakantha anyamata ace amene adakantha mfumu atate wace;

6. koma ana a ambandawo sanawapha, monga mwalembedwa m'buku la cilamulo ca Mose, m'mene adalamulira Yehova, ndi kuti, Atate asaphedwere ana, kapena ana kuphedwera atate; koma yense afere kulak wa kwa iye yekha.

7. Anapha Aedomu m'Cigwa ca Mcere zikwi khumi, nalanda Sela ndi nkhondo, naucha dzina lace Yokiteli mpaka lero lino.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 14