1. Caka caciwiri ca Yoasi mwana wa Yoahazi mfumu ya Israyeli, Amaziya mwana wa Yoasi mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.
2. Ndiye wa zaka makumi awiri ndi zisanu polowa ufumu; nakhala mfumu zaka makumi awiri mphambu zisanu ndi zinai m'Yerusalemu; dzina la mace ndiye Yoadana wa ku Yerusalemu.
3. Ndipo anacita zoongoka pamaso pa Yehova, koma wosanga Davide kholo lace; nacita monga mwa zonse anazicita Yoasi atate wace.
4. Koma misanje sanaicotsa; anthu anapherabe nsembe, nafukiza pamisanje.
5. Ndipo kunali, utakhazikika ufumu m'dzanja lace, anakantha anyamata ace amene adakantha mfumu atate wace;