Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 10:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Ahabu anali nao ana amuna makumi asanu ndi awiri m'Samariya. Nalemba akalata Yehu, natumiza ku Samariya kwa akulu a Yezreeli, ndiwo akulu akulu, ndi iwo adalera ana a Ahabu, ndi kuti,

2. Tsono akakufikani inu kalata uyu, popeza muli nao ana a mbuye wanu; muli naonso magareta ndi akavalo, ndi mudzi walinga, ndi zida,

3. musankhe wokoma ndi woyenerayo wa ana a mbuye wanu, ndi kumuika pa mpando wacifumu wa atate wace; ndipo muiponyere nkhondo nyumba ya mbuye wanu.

4. Koma anaopa kwambiri, nati, Taonani, mafumu awiri sanaima pamaso pace, nanga ife tidzaima bwanji?

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 10