Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 9:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Za aburu ako atatayika adapita masiku atatu, usalingalirenso iwowa; pakuti anapezedwa. Ndipo cifuniro conse ca Israyeli ciri kwa yani? Si kwa iwe ndi banja lonse la atate wako?

21. Ndipo Sauli anayankha nati, Sindiri Mbenjamini kodi, wa pfuko laling'ono mwa Israyeli? Ndiponso banja lathu nlocepa pakati pa mabanja onse a pfuko la Benjamini? Potero mulankhula bwanji mau otere ndi ine?

22. Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wace, napita nao ku cipinda ca alendo, nawakhalitsa pa malo a ulemu pakati pa oitanidwa onse; ndiwo anthu monga makumi atatu.

23. Ndipo Samueli ananena ndi wophika, Tenga nyama ndinakupatsa, ndi kuti, Ibakhala ndi iwe.

24. Ndipo wophikayo ananyamula mwendo ndi mnofu wace, nauika pamaso pa Sauli. Ndipo Samueli anati, Onani cimene tinakuikirani muciike pamaso panu, nudye; pakuti ici anakuikirani kufikira nthawi yonenedwa, popeza ndinati, Ndinaitana anthuwoo Comweco Sauli anadya ndi Samueli tsiku lija.

25. Ndipo pamene anatsika kumsanje kulowanso kumudzi, iye anakamba ndi Sauli pamwamba pa nyumba yace.

26. Ndipo anauka mamawa; ndipo kutaca, Samueli anaitana Sauli ali pamwamba pa nyumba, nati, Ukani kuti ndikuloleni mumuke. Ndipo Sauli anauka, naturuka onse awiri, iye ndi Samueli, kunka kunja.

27. Ndipo pamene analikutsika polekeza mudzi, Samueli ananena ndi Sauli, Uzani mnyamatayo abatsogola; napita iyeyo. Koma inu muime pano, kuti ndikumvetseni mau a Mulungu.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 9