Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 8:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Idzatenga limodzi la magawo khumi la zoweta zanu; ndipo inu mudzakhala akapoloace.

18. Ndipotsiku lija mudzapfuula cifukwa ca mfumu yanu munadzisankhira nokha; koma Yehova sadzayankha inu tsiku lijalo.

19. Koma anthu anakana kumvera mau a Samueli; nati, Iai, koma tifuna kukhala nayo mfumu yathu;

20. kuti ifenso tikafanane nao anthu a mitundu yonse; kuti mfumu yathuyo ikatiweruzire, ndi kuturuka kutitsogolera, ndi kuponya nafe nkhondo zathu.

21. Ndipo Samueli anamva mau onse a anthuwo, nawafotokozanso m'makutu a Yehova.

22. Ndipo Yehova anati kwa Samueli, Umvere mau ao, nuwalongere mfumu, Ndipo Samueli anati kwa amuna a Israyeli, Mupite, munthu yense ku mudziwace.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 8