Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 7:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Comweco anagonjetsa Afilisti, ndino iwo sanatumphanso malire a Israyeli ndipo dzanja la Yehova linasautsa Afilisti masiku onse a Samueli.

14. Ndipo midzi ya Israyeli imene Afilisti adailanda kale inabwezedwa kwa Aisrayeli, kuyambira ku Ekroni kufikira ku Gati; ndi Aisrayeli analanditsa miraga yao m'manja a Afilisti. Ndipo pakati pa Aisrayeli ndi Aamori panali mtendere;

15. ndipo Samueli anaweruza Israyeli masiku onse a moyo wace.

16. Ndipo anayenda cozungulira caka ndi caka ku Beteli, ndi ku Giligala, ndi ku Mizipa; naweruza Israyeli m'malo onse amenewa.

17. Ndipo anabwera ku Rama, pakuti nyumba yace inali kumeneko; ndipo pamenepo anaweruza Israyeli; namangapo guwa la nsembe la Yehova.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 7