19. Ndipo Mulungu anakantha anthu a ku Betisemesi, cifukwa anasuzumira m'likasa la Yehova, anakantha anthu zikwi makumi asanu; ndipo anthu analira maliro, cifukwa Yehova anawakantha anthuwo ndi makanthidwe akuru.
20. Ndipo a ku Betisemesi anati, Akhoza ndani kuima pamaso pa Yehova, Mulungu Woyera uyu? Ndipo adzakwera kwa yani pakuticokera ife?
21. Ndipo anatumiza mithenga kwa anthu a ku Kiriati-yearimu, nati, Afilisti anabwera nalo likasa la Yehova, mutsike; ndi kukwera nalo kwanu.