Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 6:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo likasa la Yehova linakhala ku dziko la Afilisti miyezi isanu ndi iwiri.

2. Ndipo Afilistiwo anaitana ansembe ndi oombeza, nati, Ticitenji ndi likasa la Yehova? mutidziwitse cimene tilitumize naco kumalo kwace.

3. Ndipo iwo anati, Ngati mulitumiza kwina likasa la Mulungu wa Israyeli, musalitumize lopanda kanthu; koma makamaka mulibweze ndi nsembe yoparamula, mukatero mudzaciritsidwa, ndi kudziwa cifukwa cace dzanja lace liri pa inu losacoka.

4. Ndipo iwo aja anati, Tidzambwezera nsembe yoparamula yanji? Ndipo iwo anati, Mafundo asanu agolidi, ndi mbewa zisanu zagolidi, monga mwa ciwerengo ca mafumu a Afilisti; popeza kusauka kumodzi kunali pa inu nonse, ndi pa mafumu anu.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 6