Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 30:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pakufika Davide ndi anthu ace ku Zikilaga tsiku lacitatu, Aamaleki adaponya nkhondo yobvumbulukira kumwera, ndi ku Zikilaga, nathyola Zikilaga nautentha ndi moto;

2. nagwira akazi ndi onse anali m'mwemo, akuru ndi ang'ono; sanapha mmodzi, koma anawatenga, namuka.

3. Ndipo pamene Davide ndi anthu ace anafika kumudziko, onani, unatenthedwa ndi moto; ndi akazi ao ndi ana ao amuna ndi akazi anatengedwa ukapolo.

4. Ndipo Davide ndi anthu amene anali naye anakweza mau ao, nalira misozi, kufikira analibe mphamvu yakuliranso.

5. Ndipo akazi awiri a Davide anatengedwa ukapolo, Ahinoamu wa ku Jezreeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli.

6. Ndipo Davide anadololoka kwambiri, pakuti anthu ananena za kumponya iye miyala, pakuti mtima wao wa anthu onse unali ndi cisoni, yense cifukwa ca ana ace amuna ndi akazi. Koma Davide anadzilimbikitsa mwa Yehova Mulungu wace.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 30