Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 3:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Tsiku lija udidzamcitira Eli zonse ndinaneneratu za pa banja lace, kuciyamba ndi kucitsiriza.

13. Popeza ndinamuuza kuti ndidzaweruza nyumba yace kosatha cifukwa ca zoipa anazidziwa, popeza ana ace anadzitengera temberero, koma iye sanawaletsa.

14. Cifukwa cace ndinalumbira kwa banja la Eli, kuti zoipa za banja la Elilo sizidzafafanizidwa ndi nsembe, kapena ndi zopereka, ku nthawi zonse.

15. Ndipo Samueli anagona kufikira m'mawa, natsegula zitseko za nyumba ya Yehova. Ndipo Samueli anaopa kudziwitsa Eli masomphenyawo.

16. Pamenepo Eli anaitana Samueli, nati, Mwana wanga, Samueli. Nati iye, Ndine.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 3