Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 23:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo Sauli anamuka mbali yina ya phiri, Davide ndi anthu ace kutseri kwace; ndipo Davide anafulumira kuthawa, cifukwa ca kuopa Sauli; popeza Sauli ndi anthu ace anazinga Davide ndi anthu ace kwete kuti awagwire.

27. Koma mthenga unafika kwa Sauli ndi kuti, Mufulumire kubwerera; popeza nkhondo yobvumbulukira ya Afilisti yalowa m'dziko.

28. Comweco Sauli anabwerera polondola Davide, nakakomana ndi Afilisti; cifukwa cace anachula dzina lace la malo aja, Thanthwe lolekanitsa.

29. Ndipo Davide anakwera kucokera kumeneko, nakhalam'ngaka za Engedi.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 23