Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 19:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo Sauli anatumiza mithengayo kuti ikaone Davide, nati, Mumtengere iye pa kama wace, kuti ndidzamuphe.

16. Ndipopakulowamithengayo, onani, pakama pali cifanizo ndi mtsamiro wa ubweya wa mbuzi kumutu kwace.

17. Nati Sauli kwa Mikala, Wandinyengeranii comweci, ndi kulola mdani wanga apulumuke? Ndipo Mikala anayankha Sauli, iye anati kwa ine, Undilole ndipite, ndingakuphe.

18. Comweco anathawa Davide, napulumuka, nafika kwa Samueli: ku Rama, namuuza zonse Sauli anamcitira. Ndipo iye ndi Samueli anakhala ku Nayoti.

19. Ndipo wina anauza Sauli, kuti, Onani Davide ali ku Nayoti m'Rama.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 19