Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 18:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo akazi anathirirana mang'ombe m'kuyimba kwao, nati,Sauli anapha zikwi zace,Koma Davide zikwi zace zankhani.

8. Koma Sauli anakwiya ndithu, ndi kunenaku kunamuipira; nati, Kwa Davide anawereogera zikwi zankhani, koma kwa ine zikwi zokha; cimperewera ncianioso, koma ufumu wokha?

9. Ndipo kuyambira tsiku lomwelo ndi m'tsogolo mwace, Sauli anakhala maso pa Davide.

10. Ndipo kunali m'mawa mwace, mzimu woipa wocokera kwa Mulungu unamgwira Sauli mwamphamvu, iye nalankhula moyaruka m'nyumba yace; koma Davide anayimba ndi dzanja lace, monga amacita tsiku ndi tsiku; koma m'dzanja la Sauli munali mkondo.

11. Ndipo Sauli anaponya mkondowo; pakuti anati, Ndidzapyoza Davide ndi kumphatikiza ndi khoma. Ndipo Davide analewa kawiri kucoka pamaso pace.

12. Ndipo Sauli anaopa Davide, cifukwa Yehova anali naye, koma adamcokera Sauli.

13. Cifukwa cace Sauli anamcotsa kuti asakhale naye, namuika akhale mtsogoleri wace wa anthu cikwi cimodzi; ndipo iye anatsogolera anthu kuturuka ndi kubwera nao.

14. Ndipo Davide anakhala wocenjera m'mayendedwe ace onse; ndipo Yehova anali naye.

15. Ndipo pamene Sauli anaona kuti analikukhala wocenjera ndithu anamuopa.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 18