Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 18:23-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo anyamata a Sauli analankhula mau awa m'makutu a Davide. Nati Davide, Kodi muciyesera cinthu copepuka kukhala mkamwini wa mfumu, popeza ndiri munthu wosauka, ndi wopeputsidwa.

24. Ndipo anyamata a Sauli anamuuza, kuti, Anatero Davide.

25. Nati Sauli, Mudzatero kwa Davide, kuti mfumu safuna colowolera cina, koma nsonga za makungu zana limodzi za Afilisti, kuti abwezere cilango adani a mfumu. Koma Sauli anaganizira kupha Davide ndi dzanja la Afilisti.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 18