Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 18:11-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Sauli anaponya mkondowo; pakuti anati, Ndidzapyoza Davide ndi kumphatikiza ndi khoma. Ndipo Davide analewa kawiri kucoka pamaso pace.

12. Ndipo Sauli anaopa Davide, cifukwa Yehova anali naye, koma adamcokera Sauli.

13. Cifukwa cace Sauli anamcotsa kuti asakhale naye, namuika akhale mtsogoleri wace wa anthu cikwi cimodzi; ndipo iye anatsogolera anthu kuturuka ndi kubwera nao.

14. Ndipo Davide anakhala wocenjera m'mayendedwe ace onse; ndipo Yehova anali naye.

15. Ndipo pamene Sauli anaona kuti analikukhala wocenjera ndithu anamuopa.

16. Koma Aisrayeli onse ndi Ayuda onse anamkonda Davide pakuti anawatsogolera kuturuka ndi kulowa nao.

17. Ndipo Sauli anati kwa Davide, Ona, mwana wanga wamkazi wamkuru, dzina lace Merabi, iyeyo ndidzakupatsa akhale mkazi wako; koma undikhalire ngwazi, nuponye nkhondo za Yehova. Pakuti Sauli anati, Dzanja langa lisamkhudze, koma dzanja la Afilisti ndilo.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 18