Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 18:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pakutsiriza iye kulankhula ndi Sauli, mtima wa Jonatani unalumikizika ndi mtima wa Davide, ndipo Jonatani anamkonda iye monga moyo wa iye yekha.

2. Ndipo Sauli anamtenga tsiku lomwelo, osamlolanso apite kwao kwa atate wace.

3. Pamenepo Jonatani ndi Davide anapangana pangano, pakuti adamkonda iye ngati moyo wa iye yekha.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 18