Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 17:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo ana atatu akuru a Jese anatsata Sauli kunkhondoko; ndi maina ao a ana ace atatuwo adapita ku nkhondowo ndiwo Eliabu woyambayo, ndi mnzace womponda pamutu pace Abinadabu, ndi wacitatu Sama.

14. Ndipo Davide anali wotsiriza; ndi akuru atatuwo anamtsata Sauli.

15. Koma Davide akamuka kwa Sauli, nabwerera kudzadyetsa nkhosa za atate wace ku Betelehemu.

16. Ndipo Mfilistiyo anayandikira m'mawa ndi madzulo, nadzionetsera masiku makumi anai.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 17