Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 16:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Cifukwa cace Sauli anatumiza mithenga kwa Jese, nati, Vnditumizire Davide, mwana wako, amene ali kunkhosa.

20. Ndipo Jese anatenga buru namsenza mkate, ndi thumba la vinyo, ndi: mwana wa mbuzi, nazitumiza kwa Sauli ndi Davide mwana wace.

21. Ndipo Davide anafika kwa Sauli, naima pamaso pace; ndipo iye anamkonda kwambiri, namsandutsa wonyamula zida zace.

22. Ndipo Sauli anatumiza kwa Jese, nati, Ulole kuti Davide aime pamaso panga; pakuti ndamkomera mtima.

23. Ndipo kunali kuti pamene mzimu woipawo wocokera kwa Mulungu unali pa Sauli, Davide anatenga zeze, naliza ndi dzanja lace; comweco Sauli anatsitsimuka, nakhala bwino, ndi mzimu woipa unamcokeraiye.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 16