Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 16:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pamenepo Samueli anatenga nyanga ya mafuta, namdzoza pakati pa abale ace; ndipo mzimu wa Yehova unalimbika pa Davide kuyambira tsiku lomweli. Ndipo Samueli ananyamuka, Danks ku Rama.

14. Koma mzimu wa Yehova unamcokera Sauli, ndi mzimu woipa wocokera kwa Yehova unambvuta iye.

15. Ndipo anyamata a Sauli ananena naye, Onani tsopano, mzimu woipa wocokera kwa Mulungu ulikubvuta inu.

16. Tsono inu mbuye wathu muuze anyamata anu, amene ali pamaso panu, kuti afune munthu wanthetemya wodziwa kuyimba zeze; ndipo kudzakhala, pamene mzimu woipa wocokera kwa Mulungu uli pa inu, iyeyo adzayimba ndi dzanja lace, ndipo mudzakhala wolama.

17. Ndipo Sauli anati kwa anyamata ace, Mundifunire tsono munthu wakudziwa kuyimba bwino, nimubwere naye kwa ine.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 16