Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 11:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Nahasi M-amoni anakwera, namanga Yabezi Gileadi zithando; ndipo anthu onse a ku Yabezi anati kwa Nahasi, Mupangane cipangano ndi ife, ndipo tidzakutumikirani inu.

2. Ndipo Nahasi Mamoni ananena nao, Ndidzapangana nanu, ngati mulola kuti maso a ku dzanja lamanja anu onse akolowoledwe; potero ndidzanyazitsa Aisrayeli onse.

3. Ndipo akuru a ku Yabezi ananena naye, Mutipatse masiku asanu ndi awiri, kuti titumize mithenga m'malire onse a Israyeli; ndipo pakapanda kuoneka wotipulumutsa ife, tidzaturukira kwa inu.

4. Tsono mithengayo inafika ku Gibeya kwa Sauli, nalankhula mau amenewa m'makutu a anthu; ndipo anthu onse anakweza mau, nalira misozi.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 11