Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 10:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Nayandikizitsa pfuko la Benjamini, banja ndi banja, ndipo banja la Amatiri linasankhidwa; nasankhidwa Sauli mwana wa Kisi. Koma pamene anamfuna, anapeza palibe.

22. Cifukwa cace anaonjeza kufunsa Yehova, Watsala wina kodi woyenera kubwera kuno? Ndipo Yehova anati, Onani, alikubisala pakati pa akatundu.

23. Ndipo anathamanga, namtenga komweko; ndipo iye pamene anaima pakati pa anthuwo, anali wamtali koposa anthu onse anamlekeza m'cifuwa.

24. Ndipo Samueli ananena ndi anthu onse, Mumuona kodi iye amene Yehova anamsankha, kuti palibe wina wakufanana naye pakati pa anthu onse? Ndipo anthu onse anapfuula, kuti, Akhale ndi moyo mfumuyo.

25. Pamenepo Samueli anafotokozera anthu macitidwe a ufumu, nawalembera m'buku, nalisunga pamaso pa Yehova. Ndipo Samueli anauza anthu onse amuke, yense ku nyumba yace,

26. Ndi Sauli yemwe anamuka ku nyumba yace ku Gibeya; ndipo am'khamu anatsagana naye iwo amene Mulungu adakhudza mitima yao.

27. Koma oipa ena anati, Uyu adzatipulumutsa bwanji? Ndipo anampeputsa, osakampatsa mtulo. Koma iye anakhala cete.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 10