Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 5:2-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti Yuda anakula mphamvu mwa abale ace, ndi mtsogoleri anafuma kwa iyeyu, koma ukulu ngwa Yosefe);

3. ana a Rubeni mwana woyamba wa Israyeli: Hanoki, ndi Palu, Hezroni, ndi Karmi.

4. Ana a Yoeli: Semaya mwana wace, Gogi mwana wace, Simei mwana wace,

5. Mika mwana wace, Reaya mwana wace, Baala mwana wace,

6. Beera mwana wace, amene Tigilati Pilesere wa ku Asuri anamtenga ndende; ndiye kalonga wa Arubeni.

7. Ndi abale ace monga mwa mabanja ao, powerenga cibadwidwe ca mibadwo yao: akuru ndiwo Yeyeli, ndi Zekariya,

8. ndi Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoeli, wokhala ku Aroeri, ndi kufikira ku Nebo ndi Baala-meoni;

9. ndi kum'mawa anakhala mpaka polowera kucipululu kuyambira mtsinje wa Firate; pakuti zoweta zao zinacuruka m'dziko la Gileadi.

10. Ndipo masiku a Sauli anagwirana nkhondo ndi Ahagiri, amene adagwa ndi dzanja lao; ndipo anakhala m'mahema mwao kum'mawa konse kwa Gileadi.

11. Ndi ana a Gadi anakhala pandunji pao m'dziko la Basana mpaka Saleka:

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 5