Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 27:8-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Kazembe wacisanu wa mwezi wacisanu ndiye Samuti M-izra; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

9. Wacisanu ndi cimodzi wa mwezi wacisanu ndi cimodzi ndiye Ira mwana wa Ikesi Mtekoi; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

10. Wacisanu ndi ciwiri wa mwezi wacisanu ndi ciwiri ndiye Helezi Mpeloni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

11. Wacisanu ndi citatu wa mwezi wacisanu ndi citatu ndiye Sibekai Mhusati wa Afera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

12. Wacisanu ndi cinai wa mwezi wacisanu ndi cinai ndiye Abiezeri M-anatoti wa Abenjamini; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

13. Wakhumi wa mwezi wakhumi ndiye Maharai Mnetofati wa Azera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

14. Wakhumi ndi cimodzi wa mwezi wakhumi ndi cimodzi ndiye Benaya Mpiratoni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

15. Wakhumi ndi ciwiri wa mwezi wakhumi ndi ciwiri ndiye Heledai Mnetofati wa Otiniyeli; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

16. Koma oyang'anira mafuko a lsrayeli ndi awa: wa Arubeni mtsogoleri wao ndiye Eliezeri mwana wa Zikiri; wa Asimeoni, Sefatiya mwana wa Maaka;

17. wa Alevi, Hasabiya mwana wa Kemueli; wa Aroni, Zadoki;

18. wa Yuda, Elihu mbale wina wa Davide; wa Isakara, Omri mwana wa Mikaeli;

19. wa Zebuluni, Isimaya mwana wa Obadiya; wa Nafitali, Yeremoti mwana wa Azrieli;

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 27