7. Wacinai wa mwezi wacinai ndiye Asebeli mbale wa Yoabu, ndi pambuyo pace Zebadiya mwana wace; ndi m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.
8. Kazembe wacisanu wa mwezi wacisanu ndiye Samuti M-izra; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
9. Wacisanu ndi cimodzi wa mwezi wacisanu ndi cimodzi ndiye Ira mwana wa Ikesi Mtekoi; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
10. Wacisanu ndi ciwiri wa mwezi wacisanu ndi ciwiri ndiye Helezi Mpeloni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
11. Wacisanu ndi citatu wa mwezi wacisanu ndi citatu ndiye Sibekai Mhusati wa Afera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
12. Wacisanu ndi cinai wa mwezi wacisanu ndi cinai ndiye Abiezeri M-anatoti wa Abenjamini; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
13. Wakhumi wa mwezi wakhumi ndiye Maharai Mnetofati wa Azera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
14. Wakhumi ndi cimodzi wa mwezi wakhumi ndi cimodzi ndiye Benaya Mpiratoni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
15. Wakhumi ndi ciwiri wa mwezi wakhumi ndi ciwiri ndiye Heledai Mnetofati wa Otiniyeli; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.
16. Koma oyang'anira mafuko a lsrayeli ndi awa: wa Arubeni mtsogoleri wao ndiye Eliezeri mwana wa Zikiri; wa Asimeoni, Sefatiya mwana wa Maaka;
17. wa Alevi, Hasabiya mwana wa Kemueli; wa Aroni, Zadoki;
18. wa Yuda, Elihu mbale wina wa Davide; wa Isakara, Omri mwana wa Mikaeli;