Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 27:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Benaya ameneyo ndiye wamphamvu uja wa makumi atatu aja, woyang'anira makumi atatu aja; woyang'anira cigawo cace ndi Amizabadi mwana wace.

7. Wacinai wa mwezi wacinai ndiye Asebeli mbale wa Yoabu, ndi pambuyo pace Zebadiya mwana wace; ndi m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

8. Kazembe wacisanu wa mwezi wacisanu ndiye Samuti M-izra; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

9. Wacisanu ndi cimodzi wa mwezi wacisanu ndi cimodzi ndiye Ira mwana wa Ikesi Mtekoi; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

10. Wacisanu ndi ciwiri wa mwezi wacisanu ndi ciwiri ndiye Helezi Mpeloni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

11. Wacisanu ndi citatu wa mwezi wacisanu ndi citatu ndiye Sibekai Mhusati wa Afera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

12. Wacisanu ndi cinai wa mwezi wacisanu ndi cinai ndiye Abiezeri M-anatoti wa Abenjamini; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 27