3. Naturutsanso anthu anali m'mwemo, nawaceka ndi mipeni ya mana mano, ndi zipangizo zocekera zacitsulo, ndi nkhwangwa. Anatero Davide ndi midzi yonse ya ana a Amoni. Ndipo Davide ndi anthu onse anabwera ku Yerusalemu.
4. Ndipo zitatha izi, inauka nkhondo ku Gezeri ndi Afilisti; pamenepo Sibekai Mhusati anapha Sipai wa ana a cimphona; ndipo anawagonjetsa.
5. Ndipo panalinso nkhondo ndi Afgisti; ndi Elihanani mwana wa Yairi anapha Lami mbale wa Goliati Mgiti, amene luti la mkondo wace linanga mtanda woombera nsaru.
6. Ndipo panalinso nkhondo ku Gati; kumeneko kunali munthu wa msinkhu waukuru, amene zala zace za kumanja ndi kumapazi ndizo makumi awiri mphambu zinai; zisanu ndi cimodzi ku dzanja liri lonse, ndi zisanu ndi cimodzi ku phazi liri lonse; nayenso anabadwa mwa cimphonaco.
7. Ndipo potonza Israyeli iyeyu Yonatani mwana wa Simeya mbale wace wa Davide anamkantha.