Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 15:9-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. a ana a Hebroni, Elieli mkuru wao, ndi abale ace makumi asanu ndi atatu;

10. a ana a Uzieli, Aminadabu mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.

11. Ndipo anaitana Zadoki ndi Abyatara ansembe, ndi Alevi Urieli, Asaya, ndi Yoeli, Semaya, ndi Elieli, ndi Aminadabu, nanena nao,

12. Inu ndinu akuru a nyumba za makolo a Alevi, mudzipatule inu ndi abale anu omwe, kuti mukatenge ndi kukwera nalo likasa la Yehova Mulungu wa Israyeli ku malo ndalikonzera.

13. Pakuti, cifukwa ca kusalinyamula inu poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anacita cotipasula, popeza sitinamfunafuma Iye monga mwa ciweruzo.

14. Momwemo ansembe ndi Alevi anadzipatula kuti akwere nalo likasa la Yehova Mulungu wa Israyeli.

15. Ndipo ana a Alevi anasenza likasa la Mulungu pa mapewa ao, mphiko ziri m'mwemo, monga Mose anawauza, monga mwa mau a Yehova.

16. Ndipo Davide ananena ndi mkuru wa Alevi kuti aike abale ao oyimbawo ndi zoyimbira, zisakasa, ndi azeze, ndi nsanje, azimveketse ndi kukweza mau ao ndi cimwemwe.

17. Ndipo Alevi anaika Hemani mwana wa Yoeli, ndi a abale ace Asafu mwana wa Berekiya, ndi a ana a Merari, abale ao, Etani mwana wa Kusaya;

18. ndi pamodzi nao abale ao a kulongosola kwaciwiri, Zekariya, Beni, ndi Yaazieli, ndi Semiramoti, ndi Yehieli, ndi Uni, Bliabu, ndi Benaya, ndi Maaseya, ndi Matitiya, ndi Blifelehu, ndi Mikineya, ndi Obedi Bdomu, ndi Yeieli, ndikirawo.

19. Oyimba tsono: Hemani, Asafu, ndi Btani, anayimba ndi nsanje zamkuwa;

20. ndi Zekariya, ndi Azieli, ndi Semiramod, ndi Yehieli, ndi Uni, ndi Bliabu, ndi Maaseya, ndi Benaya, ndi zisakasa kuyimbira mwa Alimoti;

21. ndi Matitiya, ndi Elifelehu, ndi Mikeya, ndi Obedi Edomu, ndi Yeieli, ndi Azaziya, ndi azeze akuyimbira mwa Seminiti, kutsogolera mayimbidwe.

22. Ndi Kenaniya mkuru wa Alevi anayang'anira kusenzako; anawalangiza za kusenza, pakuti anali waluso.

23. Ndi Berekiya ndi Elikana anali odikira likasa.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 15