Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 15:27-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo Davide anabvala maraya abafuta, ndi Alevi onse akunyamula likasa, ndi oyimba, ndi Kenaniya woyang'anira kusenzaku, pamodzi ndi oyimba; Davide anabvalanso efodi wabafuta.

28. Momwemo Aisrayeli onse anakwera nalo likasa la cipangano la Yehova ndi kupfuula, ndi kumveka kwa lipenga, ndi mphalasa, ndi nsanje zomveketsa, ndi zisakasa, ndi azeze.

29. Ndipo polowa likasa la cipangano la Yehova m'mudzi wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli anasuzumira pazenera, naona mfumu Davide alikutumphatumpha ndi kusewera; ndipo anampeputsa mumtima mwace.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 15