Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 14:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Maina a ana anali nao m'Yerusalemu ndi awa: Samna, ndi Sobabu Natani, ndi Solomo,

5. ndi Ibara, ndi Elisua, ndi Elipeleti,

6. ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,

7. ndi Elisama, ndi Beliyada, ndi Elifeleti.

8. Pamene Afilisti anamva kuti anamdzoza Davide akhale mfumu ya Aisrayeli onse, Afilisti onse anakwera kufunafuna Davide; ndipo Davide anamva, nawaturukira.

9. Afilisti tsono anafika, nafalikira m'cigwa ca Refaimu.

10. Ndipo Davide anafunsira kwa Mulungu, kun, Ndikwere kodi kuyambana ndi Afilisti? mudzawapereka m'dzanja langa kodi? Ndipo Yehova anati kwa iye, Kwera, pakuti ndidzawapereka m'dzanja lako.

11. Atafika tsono ku Baala Perazimu, Davide anawakantha komweko; nati Davide, Mulungu anapasula adani anga ndi dzanja langa, ngati pokhamulira madzi. Cifukwa cace analicha dzina la malowo Baala Perazimu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 14