Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 12:3-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mkuru wao ndiye Ahiezeri, ndi Yoasi, ana a Semaa wa ku Gibeya; ndi Yezieli, ndi Peleti, ana a Azmaveti; ndi Beraka, ndi Yehu wa ku Anatoti,

4. ndi Ismaya wa ku Gibeoni, wamphamvu mwa makumi atatuwo ndi woyang'anira makumi atatuwo, ndi Yeremiya, ndi Yahazieli, ndi Yohanani, ndi Yozabadi wa ku Gedera,

5. Eluzai, ndi Yerimoti, ndi Bealiya, ndi Semariya, ndi Sefatiya wa ku Harupi,

6. Elikana, ndi Isiya, ndi Azereli, ndi Yoezeri, ndi Yasobeamu ndiwo Akora;

7. ndi Yoda, ndi Zebadiya, ana a Yerohamu wa ku Gedoro.

8. Ndi Agadi ena anapambukira kwa Davide ku liogala m'cipululu, ngwazi zamphamvu zozerewera nkhondo, zogwira cikopa ndi mkondo; nkhope zao zikunga nkhope za mikango, ndi liwiro lao longa la ngoma kumapiri:

9. Ezeri mkuru wao, waciwiri Obadiya, wacitatu Eliabu,

10. wacinai Misimana, wacisanu Yeremiya,

11. wacisanu ndi cimodzi Atai, wacisanu ndi ciwiri Elieli,

12. wacisanu ndi citatu Yohanani, wacisanu ndi cinai Elzabadi,

13. wakhumi Yeremiya, wakhumi ndi cimodzi Makibanai.

14. Awa a ana a Gadi, anali atsogoleri a nkhondo; wamng'ono wa iwo anayang'anira zana limodzi, ndi wamkuru wa iwo anayang'anira cikwi cimodzi.

15. Awa ndi omwe aja anaoloka Yordano mwezi woyamba, atadzala kusefukira magombe ace onse; nathawitsa onse okhala m'zigwa kum'mawa ndi kumadzulo.

16. Ndipo anadza ena a ana a Benjamini ndi Yuda kulinga kwa Davide.

17. Ndipo Davide anaturuka kukomana nao, nayankha, nanena nao, Ngati mwandidzera mwamtendere kundithandiza, mtima wanga udzalumikizana nanu; koma ngati mwafika kundipereka kwa adani anga, popeza m'manja mwanga mulibe ciwawa, Mulungu wa makolo athu acione ndi kucilanga.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 12