39. Ndi ana a Lotani: Hori, ndi Homamu; ndipo Timna ndiye mlongo wace wa Lotani.
40. Ana a Sobala: Abiani, ndi Manahati, ndi Ebala, Sefi, ndi Oramu. Ndi ana a Zibeoni: Aiya ndi Ana.
41. Mwana wa Ana: Disoni. Ndi ana a Disoni: Hamirani, ndi Esibani, ndi Itrani, ndi Kerani.
42. Ana a Ezeri: Bilani, ndi Zavani, ndi Yakani. Ana a Disani: Uzi, ndi Arani.
43. Mafumu tsono akucita ufumu m'dziko la Edomu, pakalibe mfumu wakucita ufumu pa ana a Israyeli, ndiwo Bela mwana wa Beori; ndi dzina la mudzi wace ndilo Dinaba.
44. Ndipo anafa Bela; ndi Yobabi mwana wa Zera wa ku Bozra anakhala mfumu m'malo mwace.
45. Namwalira Yobabi; ndi Husamu wa ku dziko la Atemani anakhala mfumu m'malo mwace.
46. Namwalira Husamu; ndi Hadada mwana wa Bedadi, amene anakantha Midyani ku thengo la Moabu, anakhala mfumu m'malo mwace; ndi dzina la mudzi wace ndi Aviti.
47. Namwalira Hadada; ndi Samla wa ku Masereka anakhala mfumu m'malo mwace.
48. Namwalira Samla: ndi Sauli wa ku Rehoboti ku nyanja anakhala mfumu m'malo mwace.
49. Namwalira Sauli; ndi Baalahanani mwana wa Akiboro anakhala mfumu m'malo mwace.
50. Namwalira Baalahanani; ndi Hadada anakhala mfumu m'malo mwace; ndipo dzina la mudzi wace ndi Pai; ndi dzina la mkazi wace ndiye Mehetabele mwana wamkazi wa Matradi mwana wamkazi wa Mezahabu.
51. Namwalira Hadada. Ndipo mafumu a Edomu ndiwo mfumu Timna, mfumu Aliya, mfumu Yeteti;