Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 6:34-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. ndi zitseko ziwiri za mitengo yamlombwa pa khomo lina; panali citseko copatukana, ndi pa linzace panali citseko copatukana,

35. Ndipo analembapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nakuta zolembazo ndi golidi wopsyapsyala,

36. Ndipo bwalo la m'kati analimanga mizere itatu ya miyala yosemasema, ndi mzere umodzi wa mitanda yamkungudza.

37. Maziko ace a nyumba ya Mulungu anaikidwa m'caka cacinai m'mwezi wa Zivi.

38. Ndipo m'caka cakhumi ndi cimodzi m'mwezi wa Buli ndiwo mwezi wacisanu ndi citatu anatsiriza nyumba konse konse monga mwa mamangidwe ace onse. Momwemo anaimanga zaka zisanu ndi ziwiri.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 6