30. Ndipo anakuta ndi golidi pansi pace pa nyumba m'katimo ndi kunja.
31. Ndipo pa khomo la monenera anapanga zitseko za mtengo waazitona, citando ca khomolo cinali limodzi la magawo asanu a khoma lace.
32. Zitseko ziwiri zomwe zinali za mtengo waazitona, anasemapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nawakuta ndi golidi; inde anakutanso ndi golidi akerubi ndi migwalangwayo.
33. Momwemo anapanganso mphuthu zaazitona za pa khomo la Kacisi, citando cace cinali limodzi la magawo anai a khoma;
34. ndi zitseko ziwiri za mitengo yamlombwa pa khomo lina; panali citseko copatukana, ndi pa linzace panali citseko copatukana,
35. Ndipo analembapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nakuta zolembazo ndi golidi wopsyapsyala,