Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 6:30-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndipo anakuta ndi golidi pansi pace pa nyumba m'katimo ndi kunja.

31. Ndipo pa khomo la monenera anapanga zitseko za mtengo waazitona, citando ca khomolo cinali limodzi la magawo asanu a khoma lace.

32. Zitseko ziwiri zomwe zinali za mtengo waazitona, anasemapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nawakuta ndi golidi; inde anakutanso ndi golidi akerubi ndi migwalangwayo.

33. Momwemo anapanganso mphuthu zaazitona za pa khomo la Kacisi, citando cace cinali limodzi la magawo anai a khoma;

34. ndi zitseko ziwiri za mitengo yamlombwa pa khomo lina; panali citseko copatukana, ndi pa linzace panali citseko copatukana,

35. Ndipo analembapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nakuta zolembazo ndi golidi wopsyapsyala,

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 6