Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 6:25-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndi kerubi winayo msinkhu wace unali mikono khumi; akerubi onse awiri anafanana muyeso wao ndi msinkhu wao.

26. Msinkhu wa kerubi mmodzi unali mikono khumi, ndi wa kerubi wina momwemo.

27. Ndipo anaika akerubiwo m'cipinda ca m'katimo, ndi mapiko a akerubiwo anatambasuka kotero kuti phiko lace la kerubi mmodzi linajima ku khoma limodzi, ndipo phiko la kerubi wina linajima khoma lina, ndi mapiko ao anagundana pakati pa nyumba.

28. Ndipo anawakuta akerubi ndi golidi.

29. Nalemba m'makoma onse akuzinga cipinda mafano olemba ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, m'katimo ndi kumbuyo kwace.

30. Ndipo anakuta ndi golidi pansi pace pa nyumba m'katimo ndi kunja.

31. Ndipo pa khomo la monenera anapanga zitseko za mtengo waazitona, citando ca khomolo cinali limodzi la magawo asanu a khoma lace.

32. Zitseko ziwiri zomwe zinali za mtengo waazitona, anasemapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nawakuta ndi golidi; inde anakutanso ndi golidi akerubi ndi migwalangwayo.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 6