Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 4:7-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo Solomo anali nao akapitao khumi ndi awiri akuyang'anira Aisrayeli onse, akufikitsira mfumu ndi banja lace zakudya; ali yense anafikitsa zakudya zofikira mwezi umodzi wa caka.

8. Ndipo maina ao ndiwo: Benhuri anatengetsa ku mapiri a Efraimu;

9. Bendekeri ku Makazi ndi Saalibimu ndi Betsemesi ndi Elonibetanani;

10. Benhesedi ku Aruboti ndi Soko ndi dziko lonse la Heferi;

11. Benabinadabu ku mtunda wa Dori, mkazi wace ndiye Tafati mwana wa Solomo;

12. Baana mwana wa Ahiludi ku Tanaki ndi Megido ndi Betseani konse, ali pafupi ndi Zaratana kunsi kwa Yezreeli, kuyambira ku Betseani kufikira ku Abelimehola, kufikiranso kundunji ku Yokineamu;

13. Benigeheri ku Ramoti Gileadi, iyeyo anali nayo midzi ya Yairo mwana wa Manase iri m'Gileadiyo, iye anali nalo dziko la Arigobi liri m'Basani, midzi yaikuru makumi asanu ndi limodzi yamalinga ndi zitseko zamkuwa;

14. Abinadabu mwana wa Ido ku Nahanaimu;

15. Ahimazi ku Nafitali, iyeyu adakwatira Basemati mwana wa Solomo;

16. Baana mwana wa Husayi ku Aseri ndi ku Aloti;

17. Yehosafati mwana wa Paruwa ku Isakara;

18. Simeyi mwana wa Ela ku Benjamini;

19. Geberi mwana wa Uri ku dziko la Gileadi, dziko la Sihoni mfumu ya Aamori, ndi la Ogi mfumu ya Basani; munalibe kapitao wina m'deramo.

20. Ayuda ndi Aisrayeli anacuruka ngati mcenga wa kunyanja, namadya namamwa namakondwera.

21. Ndipo Solomo analamulira maiko onse, kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti ndi ku malire a Aigupto; anthu anabwera nayo mitulo namtumikira Solomo masiku onse a moyo wace.

22. Ndipo zakudya za Solomo zofikira tsiku limodzi zinalr miyeso makumi atatu ya ufa wosalala, ndi miyeso makumi asanu ndi limodzi ya ufa wamankhupete,

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 4