Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 4:29-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo Mulungu anampatsa Solomo nzeru ndi luntha lambiri, ndi mtima wodziwa za mitundu mitundu, zonga mcenga uli m'mbali mwa nyanja.

30. Ndipo nzeru ya Solomo inaposa nzeru za anthu onse a kum'mawa, ndi nzeru zonse za ku Aigupto.

31. Pakuti anali wanzeru woposa anthu onse, woposa Etani wa ku Ezra, ndi Hemani, ndi Kalikoli, ndi Darida ana a Maholi; ndipo mbiri yace inafikira amitundu onse ozungulira.

32. Ndipo ananena miyambo zikwi zitatu, ndipo nyimbo zace zinali cikwi cimodzi mphambu zisanu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 4