Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 3:25-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Mfumu niti, Dula pakati mwana wamoyoyu, nupatse mmodzi cipinjiri, ndi wina cipinjiri cace.

26. Koma mkazi amene mwana wamoyo anali wace analankhula ndi mfumu, popeza mtima wace unalira mwana wace, nati, Ha! mbuye wanga, mumpatse uyo mwana wamoyo osamupha konse. Koma winayo anati, Asakhale wanga kapena wako, dulani.

27. Pamenepo mfumu inayankha, niti, Mumpatse wacifundoyo mwana wamoyo, osamupha konse, uyo ndiye amace.

28. Ndipo Aisrayeli onse anamva maweruzidwe ace idaweruza mfumu, naopa mfumu; pokhala anaona kuti nzeru ya Mulungu inali mwa iye yakuweruza.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 3